Chirichonse chimene Mulungu amachipanga, amachipanga mwapamwamba kwambiri. Kuchita zinthu kwa Mulungu mwapamwamba kwambiri kunaonekera pa Genesis mutu woyamba pamene analenga ndipo kenako ndikuyesa ntchito za manja ake omwe ndipo analengeza kuti zinali zabwino.
• Chingwe chamapando – mizera imakhala yoongoka komanso mipata yolondola.
• Zikhomo zamuyaya – kubyala m’mapando omwewo chaka ndi chaka.
• Mapando - amakhala masentimita 60 ndi 75, ndipo kuya molingana ndi zothirapo.
• Kubyala – mbeu zitatu pa mzere kunsi kwa phando lanu.
• Ndipo pamakhala mbeu zochuluka 44,444 za chimanga mutatha kupatulira.
• Munda ukuyenera kupaliridwa chaka chonse kuti musakhale udzu.
• Munda ukuyenera kuvindikiridwa onse ndi bulangeti la Mulungu.
• Kuthira bwino kwa fetereza ndi manyowa komanso mbeu.
Zifukwa zobyalira pa phando lomwero chaka ndi chaka:
• Zakudya za mbeu zimene zinatsala chaka chatha zimagwiritsidwa ntchito ndi mbeu ya chaka chotsatira.
• Dothi limayamba kufewa komanso limakhweka pogwiritsa ntchito.
• Mizu yovunda ya mbeu ya chaka chatha imaonjezera chonde ndipo imasiya mauna kuti mizu ina izikula mosavuta komanso kuti madzi adzilowa bwino pansi.
• Kugogomezeka kwa dothi kumachitika pakatikati pa mizere basi.
• Kusatembenuzidwa kwa dothi pakati pa mbeu kumapangitsa kuti udzu usamere ochuluka ai.
Mulingo wina uliwonse wakuchita mwapamwamba kwambiri ulipo kuti utichitire ubwino osati chifukwa chakuchita mwa ngwiro ai. Milingo imeneyi inasankhidwa mosamala bwino kuti minda yathu ikapeze phindu.
• Akolose 3:23 “ chiri chonse chimene muchita, chitani ndi mtima onse, ngati kwa Ambuye osati kwa munthu ai.”