Mu Baibulo, chitsanzo chabwino chokuti Yesu samataya kanthu chikuoneka pamene Iye anadyetsa amuna zikwi zisanu 

(Mateyu 14:14) 

Zitsanzo za Mulungu zosataya kanthu: 

• Mzungulire wa madzi 

• Mzungulire wa Kaboni 

Kutaya kwa munthu: 

• Kugwetsa nkhalango mwachisawawa 

• Ulimi wochetcha ndi kuotcha 

• Kukokololoka kwa dothi 

• Kuthamanga kwa madzi 

• Kulima minda yaikulu popanda phindu ndi kutaya 

Kulima mu Njira ya Mulungu kumaonetsetsa kuti pasakhale kutaya kanthu pa madera awa: 

• Kusafuna kupeza malo ena olima chifukwa zokolola zimachuluka pa malo omwewo muli nawo. 

• Mumateteza nthaka 

• Mvula imalowa pansi 

• Kuthamanga kwa madzi kumachepetsedwa 

• Mumateteza chinyezi 

• Chonde chimachuluka munthaka kupyolera mkuzungulira kwa zakudya za mbeu muchirengedwe 

• Mbeu zimapanga m’thunzi mwachangu 

• Zothira m’mapando zimagwira ntchito moyenera 

• Nthawi komanso ndalama zimasungidwa